5 Kunena za nthaka, kucokera momwemo mumaturuka cakudya,Ndi m'munsi mwace musandulizika ngati ndi moto.
6 Miyala yace ndiyo malo a safiro,Ndipo iri nalo pfumbi lagolidi.
7 Njira imeneyi palibe ciombankhanga ciidziwa;Lingakhale diso la kabawi losapenyapo.
8 Nyama zodzikuza sizinapondapo,Ngakhale mkango waukali sunapitapo.
9 Munthu atambasulira dzanja lace kumwala;Agubuduza mapiri kuyambira kumizu.
10 Asema njira pakati pa matanthwe,Ndi diso lace liona ciri conse ca mtengo wace.
11 Atseka mitsinje ingadonthe;Naturutsira poyera cobisikaci.