1 Ndipo Yobu anaonjezanso mwambi wace, nati,
2 Ha! ndikadakhala monga m'miyezi yapitayi,Monga m'masiku akundisunga Mulungu;
3 Muja nyali yace inawala pamutu panga,Ndipo ndi kuunika kwace ndinayenda mumdima;
4 Monga umo ndinakhala m'masiku anga olimba,Muja uphungu wa Mulungu unakhala pahema panga;