2 Ha! ndikadakhala monga m'miyezi yapitayi,Monga m'masiku akundisunga Mulungu;
3 Muja nyali yace inawala pamutu panga,Ndipo ndi kuunika kwace ndinayenda mumdima;
4 Monga umo ndinakhala m'masiku anga olimba,Muja uphungu wa Mulungu unakhala pahema panga;
5 Muja Wamphamvuyonse akali nane pamodzi,Ndi ana anga anandizinga;
6 Muja popondera ine padakhatamira ndi mafuta amkaka,Ndi thanthwe linanditsanulira mitsinje ya mafuta aazitona!
7 Muja ndinaturuka kumka kucipata kumudzi,Muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,
8 Anyamata anandiona nabisala,Okalamba anandinyamukira, nakhala ciriri,