8 Anyamata anandiona nabisala,Okalamba anandinyamukira, nakhala ciriri,
9 Akalonga anadziletsa kulankhula,Ndi kugwira pakamwa pao;
10 Mau a omveka anali zi,Ndi lilime lao linamamatira ku malakalaka ao.
11 Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa;Ndipo pondiona diso, linandicitira umboni.
12 Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakupfuula;Mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.
13 Dalitso la iye akati atayike linandidzera,Ndi mtima wa mkazi wamasiye ndinauyimbitsa mokondwera.
14 Ndinabvala cilungamo, ndipo cinandibvala ine;Ciweruzo canga cinanga mwinjiro ndi nduwira.