1 Atatero, Yobu anatsegula pakamwa pace, natemberera tsiku lace.
2 Nalankhula Yobu nati,
3 Litayike tsiku lobadwa ine,Ndi usikuwo udati, Waima naye mwana wamwamuna.
4 Tsiku lija likhale mdima;Mulungu asalifunse kumwamba,Ndi kuunika kusaliwalire.