1 Atatero, Yobu anatsegula pakamwa pace, natemberera tsiku lace.
2 Nalankhula Yobu nati,
3 Litayike tsiku lobadwa ine,Ndi usikuwo udati, Waima naye mwana wamwamuna.
4 Tsiku lija likhale mdima;Mulungu asalifunse kumwamba,Ndi kuunika kusaliwalire.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa ziliyese lao lao;Mtambo ulikhalire;Zonse zodetsa usana bi ziliopse.
6 Usiku uja, mdima weni weni uugwere;Usakondwerere mwa masiku a m'caka;Usalowe m'ciwerengedwe ca miyezi.
7 Ha! usiku uja ukhale cumba;Kuyimbira kokondwera kusalowem'mwemo.