5 Mdima ndi mthunzi wa imfa ziliyese lao lao;Mtambo ulikhalire;Zonse zodetsa usana bi ziliopse.
6 Usiku uja, mdima weni weni uugwere;Usakondwerere mwa masiku a m'caka;Usalowe m'ciwerengedwe ca miyezi.
7 Ha! usiku uja ukhale cumba;Kuyimbira kokondwera kusalowem'mwemo.
8 Autemberere iwo akutemberera usana,Odziwa kuutsa cinjokaco.
9 Nyenyezi za cizirezire zide;Uyembekezere kuunika, koma kuusowe;Usaone kuphenyuka kwa mbanda kuca;
10 Popeza sunatseka pa makomo ace mimba ya mai wanga.Kapena kundibisira mabvuto pamaso panga.
11 Ndinalekeranji kufera m'mimba?Ndi kupereka mzimu wanga pobadwa ine?