31 Ngati amuna a m'hema mwanga sanati,Ndani adzapeza munthu wosakhuta nyama yomgawira Yobu?
32 Mlendo sakagona pakhwalala,Koma ndinatsegulira wam'njira pakhomo panga.
33 Ngati ndakwirira zolakwa zanga monga Adamu,Ndi kubisa mphulupulu yanga m'cifuwa mwanga;
34 Popeza ndinaopa unyinji waukuru,Ndi cipepulo ca mapfuko cinandiopsetsa;Potero ndinakhala cete osaturuka pakhomo panga.
35 Ha! ndikadakhala naye wina wakundimvera,Cizindikilo canga sici, Wamphamvuyonse andiyankhe;Mwenzi ntakhala nao mau akundineneza analemberawo mdani wangal
36 Ndithu ndikadawasenza paphewa panga,Ndi kudzimangirira awa ngati korona.
37 Ndikadamfotokozera ciwerengo ca mopondamo mwanga,Ndikadamsenderera Iye ngati ka longa,