32 Mlendo sakagona pakhwalala,Koma ndinatsegulira wam'njira pakhomo panga.
33 Ngati ndakwirira zolakwa zanga monga Adamu,Ndi kubisa mphulupulu yanga m'cifuwa mwanga;
34 Popeza ndinaopa unyinji waukuru,Ndi cipepulo ca mapfuko cinandiopsetsa;Potero ndinakhala cete osaturuka pakhomo panga.
35 Ha! ndikadakhala naye wina wakundimvera,Cizindikilo canga sici, Wamphamvuyonse andiyankhe;Mwenzi ntakhala nao mau akundineneza analemberawo mdani wangal
36 Ndithu ndikadawasenza paphewa panga,Ndi kudzimangirira awa ngati korona.
37 Ndikadamfotokozera ciwerengo ca mopondamo mwanga,Ndikadamsenderera Iye ngati ka longa,
38 Ngati minda yanga ipfuula monditsutsa,Ndi nthumbira zace zilira pamodzi;