4 Nanga sapenyanjira zanga,Ndi kuwerenga moponda mwanga monse?
5 Ngati ndinayanjana nalo bodza,Ndi phazi langa linathamangira cinyengo;
6 Andiyese ndi muyeso wolingana,Kuti Mulungu adziwe ungwiro wanga.
7 Ngati phazi langa linapambuka m'njira,Ndi mtima wanga unatsata maso anga?Ngati cirema camamatira manja anga?
8 Ndibzale ine nadye wina,Ndi zondimerera ine zizulidwe.
9 Ngati mtima wanga wakopeka ndi mkazi,Ngati ndalalira pa khomo la mnzanga,
10 Mkazi wanga aperere wina;Wina namuike kumbuyo.