12 Inde ndinasamalira inu;Koma taonani, panalibe womtsutsa Yobu,Kapena wakumbwezera mau pakati painu.
13 Msamati, Tapeza nzeru ndife,Mulungu akhoza kumkhulula, si munthu ai;
14 Popeza sanandiponyera ine mau,Sindidzamyankha ndi maneno anu.
15 Asumwa, sayankhanso, Anawathera mau.
16 Kodi ndidzangolindira popeza sanena iwo,Popeza akhala du osayankhanso?
17 Ndidzayankha inenso mau anga,Ndidzaonetsa inenso za m'mtima mwanga.
18 Pakuti ndadzazidwa ndi mau,Ndi mzimu wa m'kati mwanga undifulumiza.