5 Koma pakuona Elihu kuti anthu atatuwa anasowa poyankha pakamwa pao anapsa mtima.
6 Ndipo Elihu mwana wa Barakeli wa ku Buzi anayankha, nati,Ine ndine mnyamata, inu ndinu okalamba;Cifukwa cace ndinadziletsa, ndi kuopa kukuonetsani monga umo ndayesera ine.
7 Ndinati, Amisinkhu anene,Ndi a zaka zocuruka alangize nzeru.
8 Koma m'munthu muli mzimu,Ndi mpweya wa Wamphamvuyonse wawazindikiritsa.
9 Akulu sindiwo eni nzeru,Ndi okalamba sindiwo ozindikira ciweruzo.
10 Cifukwa cace ndinati, Ndimvereni ine,Inenso ndidzaonetsa monga umo ndayesera ine.
11 Taonani, ndinalindira mau anu,Ndinacherera khutu zifukwa zanu,Pofunafuna inu ponena.