12 Taonani, ndidzakuyankhani m'mene muli mosalungama;Pakuti Mulungu ndiye wamkulu woposa munthu.
13 Mutsutsana ndi Iye cifukwa ninji?Popeza pa zace zonse saulula cifukwa.
14 Pakuti Mulungu alankhula kamodzi,Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.
15 M'kulota, m'masomphenya a usiku,Pakuwagwera anthu tulo tatikuru,Pogona mwacheru pakama,
16 Pamenepo atsegula makutu a anthu,Nakomera cizindikilo cilangizo cao;
17 Kuti acotse munthu ku cimene akadacita,Ndi kubisira munthu kudzikuza kwace;
18 Kuti amletse angaonongeke,Ndi moyo wace ungatayike ndi lupanga.