14 Pakuti Mulungu alankhula kamodzi,Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.
15 M'kulota, m'masomphenya a usiku,Pakuwagwera anthu tulo tatikuru,Pogona mwacheru pakama,
16 Pamenepo atsegula makutu a anthu,Nakomera cizindikilo cilangizo cao;
17 Kuti acotse munthu ku cimene akadacita,Ndi kubisira munthu kudzikuza kwace;
18 Kuti amletse angaonongeke,Ndi moyo wace ungatayike ndi lupanga.
19 Alangidwanso ndi zowawa pakama pace,Ndi kulimbana kowawa kosapuma m'mafupa ace.
20 M'mwemo mtima wace ucita mseru ndi mkate,Ndi moyo wace pa cakudya colongosoka.