20 M'mwemo mtima wace ucita mseru ndi mkate,Ndi moyo wace pa cakudya colongosoka.
21 Mnofu wace udatha, kuti sungapenyeke;Ndi mafupa ace akusaoneka aturuka.
22 Inde wasendera kufupi ku manda,Ndi moyo wace kwa akuononga.
23 Akakhala kwa iye mthenga,Womasulira mau mmodzi mwa cikwi,Kuonetsera munthu comuyenera;
24 Pamenepo Mulungu amcitira cifundo, nati,Mlanditse, angatsikire kumanda,Ndampezera dipo.
25 Mnofu wace udzakhala se, woposa wa mwana;Adzabwerera ku masiku a ubwana wace.
26 Apembedza Mulungu, ndipo amkomera mtima;M'mwemo aona nkhope yace mokondwera;Ndipo ambwezera munthu cilungamo cace.