4 Mzimu wa Mulungu unandilenga,Ndi mpweya wa Wamphamvuyonse umandipatsa moyo.
5 Ngati mukhoza, mundiyankhe;Mulongosolere mau anu pamaso panga, mukonzeke.
6 Taonani, ndikhala kwa Mulungu ngati inu;Inenso ndinaumbidwa ndi dothi,
7 Taonani, kuopsa kwanga simudzacita nako mantha;Ndi ici ndikusenzetsani sicidzakulemererani.
8 Zedi mwanena m'makutu mwanga,Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,
9 Ndine woyera ine, wopanda kulakwa,Ndine wosaparamula, ndiribe mphulupulu.
10 Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo,Andiyesa mdani wace;