6 Taonani, ndikhala kwa Mulungu ngati inu;Inenso ndinaumbidwa ndi dothi,
7 Taonani, kuopsa kwanga simudzacita nako mantha;Ndi ici ndikusenzetsani sicidzakulemererani.
8 Zedi mwanena m'makutu mwanga,Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,
9 Ndine woyera ine, wopanda kulakwa,Ndine wosaparamula, ndiribe mphulupulu.
10 Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo,Andiyesa mdani wace;
11 Amanga mapazi anga m'zigologolo,Ayang'anira poyenda ine ponse.
12 Taonani, ndidzakuyankhani m'mene muli mosalungama;Pakuti Mulungu ndiye wamkulu woposa munthu.