8 Zedi mwanena m'makutu mwanga,Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,
9 Ndine woyera ine, wopanda kulakwa,Ndine wosaparamula, ndiribe mphulupulu.
10 Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo,Andiyesa mdani wace;
11 Amanga mapazi anga m'zigologolo,Ayang'anira poyenda ine ponse.
12 Taonani, ndidzakuyankhani m'mene muli mosalungama;Pakuti Mulungu ndiye wamkulu woposa munthu.
13 Mutsutsana ndi Iye cifukwa ninji?Popeza pa zace zonse saulula cifukwa.
14 Pakuti Mulungu alankhula kamodzi,Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.