1 Ndipo Elihu anabwereza kunena, nati,
2 Tamverani mau anga, inu anzeru;Mundicherere khutu inu akudziwa.
3 Pakuti khutu liyesa mau,Monga m'kamwa mulawa cakudya.
4 Tidzisankhire coyeneraco,Tidziwe mwa tokha cokomaco.
5 Pakuti Yobu wanena, Ine ndine wolungama,Ndipo Mulungu wandicotsera coyenera ine.
6 Kodi ndidzinamizire?Bala langa nlosapola, ngakhale sindinalakwa.