16 Inde akadakukopani mucoke posaukira,Mulowe kucitando kopanda copsinja;Ndipo zoikidwa pagome panu zikadakhala zonona ndithu.
17 Koma mukadzazidwa nazo zolingirira oipa,Zolingirirazo ndi ciweruzo zidzakugwiranibe,
18 Pakuti mucenjere, mkwiyo ungakunyengeni mucite mnyozo;Ndipo usakusokeretseni ukulu wa dipoli.
19 Cuma canu cidzafikira kodi, kuti simudzakhala wopsinjika,Kapena mphamvu yanu yonse yolimba?
20 Musakhumbe usiku,Umene anthu alikhidwe m'malo mwao.
21 Cenjerani, musaluniike kumphulupulu;Pakuti mwaisankha iyi mutazunzidwa.
22 Taonani, Mulungu acita mokwezeka mu mphamvu yace,Mphunzitsi wakunga Iye ndani?