6 Sasunga woipa akhale ndi moyo,Koma awaninkha ozunzikazowayenera iwo.
7 Sawacotsera wolungama maso ace,Koma pamodzi ndi mafumu pa mpando waoAwakhazika cikhazikire, ndipo akwezeka.
8 Ndipo akamangidwa m'nsinga,Nakakodwa ndi zingwe za mazunzo,
9 Pamenepo awafotokozera nchito zao,Ndi zolakwa zao, kuti anacita modzikuza.
10 Awatseguliranso m'khutu mwao kuti awalangize,Nawauza abwerere kuleka mphulupulu.
11 Akamvera ndi kumtumikira,Adzatsiriza masiku ao modala,Ndi zaka zao mokondwera.
12 Koma akapanda kumvera adzatayika ndi lupanga,Nadzatsirizika osadziwa kanthu.