1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,
2 Munthu akayesa kunena nawe mau, kodi udzamva nao cisoni?Koma akhoza ndani kudziletsa kunena?
3 Taona iwe walangiza aunyinji,Walimbitsa manja a ofoka.
4 Mau ako anacirikiza iye amene akadagwa,Walimbitsanso maondo otewa.
5 Koma tsopano cakufikira iwe, ndipo ukomoka;Cikukhudza, ndipo ubvutika.