13 M'malingaliro a masomphenya a usiku,Powagwira anthu tulo tatikuru,
14 Anandidzera mantha ndi kunjenjemera,Nanthunthumira nako mafupa anga onse.
15 Pamenepo panapita mzimu pamaso panga;Tsitsi la thupi langa lidati nyau nyau.
16 Unaima ciriri, koma sindinatha kuzindikira maonekedwe ace;Panali mzukwa pamaso panga;Kunali cete, ndipo ndidamva mau akuti,
17 Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu?Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wace?
18 Taona, sakhulupirira atumiki ace;Nawanenera amithenga ace zopusa;
19 Kopambana kotani nanga iwo akukhala m'nyumba zadothi,Amene kuzika kwao kuti m'pfumbi,Angothudzulidwa ngati gulugufe,