17 Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu?Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wace?
18 Taona, sakhulupirira atumiki ace;Nawanenera amithenga ace zopusa;
19 Kopambana kotani nanga iwo akukhala m'nyumba zadothi,Amene kuzika kwao kuti m'pfumbi,Angothudzulidwa ngati gulugufe,
20 Kuyambira m'mawa kufikira madzulo athudzuka;Aonongeka kosatha, osasamalirako munthu.
21 Kukometsetsa kwao sikumacotsedwa nao?Amafa koma opanda nzeru.