4 Mau ako anacirikiza iye amene akadagwa,Walimbitsanso maondo otewa.
5 Koma tsopano cakufikira iwe, ndipo ukomoka;Cikukhudza, ndipo ubvutika.
6 Kodi kulimbika mtima kwako si ndiko kuti uopa Mulungu,Ndi ciyembekezo cako si ndiwo ungwiro wa njira zako?
7 Takumbukila tsopano, watayika ndani wosaparamula konse?Kapena oongoka mtima alikhidwa kuti?
8 Monga umo ndaonera, olimira mphulupulu,Nabzala bvuto, akololapo zomwezo.
9 Atayika ndi mpweya wa Mulungu,Nathedwa ndi mpumo wa mkwiyo wace.
10 Kubangula kwa mkango, ndi kulira kwa mkango waukali kwaletsedwa,Ndi mano a misona ya mkango atyoledwa.