1 Ndipo Yehova anabwereza kwa Yobu, nati,
2 Kodi wodzudzulayo atsutsane ndi Wamphamvuyonse?Wocita makani ndi Mulungu ayankhe.
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova, nati,
4 Taonani, ndakhululuka ine, ndidzakubwezerani mau otani?Ndigwira pakamwa.