2 Kodi wodzudzulayo atsutsane ndi Wamphamvuyonse?Wocita makani ndi Mulungu ayankhe.
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova, nati,
4 Taonani, ndakhululuka ine, ndidzakubwezerani mau otani?Ndigwira pakamwa.
5 Ndalankhula kamodzi, koma sindidzayankha;Inde kawiri, koma sindionjezanso.
6 Ndipo Yehova anamyankha Yobu m'kabvumvulu, nati,
7 Dzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna;Ndidzakufunsa, undidziwitse.
8 Cingakhale ciweruzo canga udzacityola kodi?Udzanditsutsa kuti ndiri woipa kodi, kuti ukhale wolungama ndiwe?