5 Ndalankhula kamodzi, koma sindidzayankha;Inde kawiri, koma sindionjezanso.
6 Ndipo Yehova anamyankha Yobu m'kabvumvulu, nati,
7 Dzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna;Ndidzakufunsa, undidziwitse.
8 Cingakhale ciweruzo canga udzacityola kodi?Udzanditsutsa kuti ndiri woipa kodi, kuti ukhale wolungama ndiwe?
9 Kodi uli nalo dzanja ngati Ine Mulungu?Kapena ukhoza kugunda ndi mau ngati Ine?
10 Udzikometsere tsono ndi ukulu ndi kukuzika,Nubvale ulemu ndi ulemerero.
11 Tsanulira mkwiyo wako wosefuka,Nupenyerere ali yense wodzikuza ndi kumcepetsa,