4 Kodi idzapangana ndi iwe,Kuti uitenge ikhale kapolo wako wacikhalire?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame?Kapena udzaimangira anamwali ako kuti aiwete?
6 Kodi opangana malonda adzaitsatsa?Adzaigawana eni malonda?
7 Kodi udzadzaza khungu lace ndi nchetho,Kapena mutu wace ndi miomba?
8 Isanjike dzanja lako;Ukakumbukila nkhondoyi, sudzateronso.
9 Taona, ciyembekezo cako ca pa iyo cipita pacabe.Kodi sadzatenga nkhawa munthu pakungoiona?
10 Palibe wolimba mtima kuti adzaiputa.Ndipo ndaniyo adzaima pamaso pa Ine?