7 Koma munthu abadwira mabvuto,Monga mbaliwali zikwera ziuluzika.
8 Koma ine ndikadafuna Mulungu,Ndikadaikira mlandu wanga Mulungu;
9 Amene acita zazikuru ndi zosalondoleka,Zinthu zodabwiza zosawerengeka.
10 Amene abvumbitsa mvula panthaka,Natumiza madzi paminda;
11 Kuika opeputsidwa pamalo ponyamuka,Kuti iwo a maliro akwezedwe posatekeseka.
12 Apititsa pacabe ziwembu za ocenjerera,Kuti manja ao sakhoza kucita copangana cao.
13 Akola eni nzeru m'kucenjerera kwao,Ndi uphungu wa opotoka mtima usonthokera pacabe,