24 Mundilangize, ndipo ndidzakhala cete ine;Mundizindikiritse umo ndinalakwira.
25 Mau oongoka si ndiwo amphamvu?Koma kudzudzula kwanu mudzudzula ciani?
26 Kodi muyesa kudzudzula mau?Popeza maneno a munthu wodololoka akunga mphepo.
27 Indetu, mugwetsera wamasiye msampha,Mumkumbira bwenzi lanu mbuna.
28 Koma tsopano balindani, mundipenyerere;Ndikanena bodza pamaso panu mudzalizindikira.
29 Bwererani, ndikupemphani, musandiipsire mlandu;Inde, bwereraninso, mlandu wanga ngwolungama.
30 Kodi pali cosalungama palilime panga?Ngati sindizindikira zopanda pace m'kamwa mwanga?