8 Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha,Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!
9 Cimkomere Mulungu kundiphwanya,Alole dzanja lace lindilikhel
10 Pamenepo ndidzasangalala,Ndidzakondwera naco cowawa cosandileka;Pakuti sindinawabisa mau a Woyerayo.
11 Mphamvu yanga njotani kuti ndiyembekeze?Mathedwe anga ndi otani kuti ndipirire?
12 Kodi mphamvu yanga ndiyo mphamvu ya miyala?Mnofu wanga ndi mkuwa kodi?
13 Mulibe thandizo mwa ine ndekha; cipulumutso candithawa.
14 Iye amene akadakomoka, bwenzi lace ayenera kumcitira cifundo;Angaleke kuopa Wamphamvuyonse.