1 Kodi munthu alibe nkhondo kunja kuno?Kodi masiku ace sakunga masiku a wolembedwa nchito?
2 Monga kapolo woliralira mthunzi,Monga wolembedwa nchito ayembekezera mphotho yace,
3 Momwemo anandilowetsa miyezi yopanda pace.Nandiikiratu zowawa usiku ndi usiku.
4 Ndigona pansi, ndikuti,Ndidzauka liti? koma usiku undikulira;Ndipo ndimapalapata mpaka mbanda kuca.