10 Sadzabweranso ku nyumba yace,Osamdziwanso malo ace.
11 Potero sindidzaletsa pakamwa panga;Ndidzalankhula popsinjika mumzimu mwanga;Ndidzadandaula pakuwawa mtima wanga.
12 Ndine nyanja kodi, kapena cinjoka ca m'nyanja,Kuti Inu mundiikira odikira?
13 Ndikati, Pakama panga mpondisangalatsa,Pogona panga padzacepsa condidandaulitsa;
14 Pamenepo mundiopsa ndi maloto,Nimundicititsa mantha ndi masomphenya;
15 Potero moyo wanga usankha kupotedwa,Ndi imfa, koposa mafupa anga awa.
16 Ndinyansidwa nao moyo wanga; sindidzakhala ndi moyo cikhalire;Mundileke; pakuti masiku anga ndi acabe.