15 Adzatsamira nyumba yace, koma yosamlimbira;Adzaiumirira koma yosakhalitsa.
16 Akhala wamuwisi pali dzuwa,Ndi nthambi zace ziturukira pamunda pace.
17 Mizu yace iyangayanga pa kasupe wamadzi,Apenyerera pokhalapo miyala.
18 Akamuononga kumcotsa pamalo pace,Padzamkana, ndi kuti, Sindinakuona.
19 Taona, ici ndico comkondweretsa panjira pace,Ndi panthaka padzamera ena.
20 Taona, Mulungu sakana munthu wangwiro;Kapena kugwiriziza ocita zoipa.
21 Koma adzadzaza m'kamwa mwako ndi kuseka,Ndi milomo yako kupfuula.