7 Ndipo cinkana ciyambi cako cinali cacing'ono,Citsiriziro cako cidzacuruka kwambiri.
8 Pakuti ufunsire tsono mbadwo wapitawo,Nusamalire zimene makolo ao adazisanthula;
9 Pakuti ife ndife adzulo, osadziwa kanthu,Popeza masiku athu a pa dziko lapansi ndiwo ngati mthunzi;
10 Amene aja sangakuphunzitse, ndi kukufotokozera,Ndi kuturutsa mau a mumtima mwao?
11 Ngati gumbwa aphuka popanda cinyontho?Ngati mancedza amera popanda madzi?
12 Akali auwisi, sanawaceka,Auma, asanaume mathengo onse ena.
13 Momwemo mayendedwe a onse oiwala Mulungu;Ndi ciyembekezo ca onyoza Mulungu cidzatayika;