1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,
2 Zoona, ndidziwa kuti ciri cotero.Koma munthu adzakhala walungama bwanji kwa Mulungu?
3 Akafuna Iye kutsutsana naye,Sadzambwezera Iye mau amodzi onse mwa cikwi.
4 Ndiye wa mtima wanzeru, ndi wa mphamvu yaikuru;Ndaniyo anadziumitsa mtima pa Iye, nakhala nao mtendere?