13 Mulungu sadzabweza mkwiyo wace;Athandizi odzikuza awerama pansi pa Iye.
14 Nanga ine tsono ndidzamyankha bwanji,Ndi kusankha mau anga akutsutsana ndi Iye?
15 Ameneyo, cinkana ndikadakhala wolungama, sindikadamyankha; Ndikadangompembedza wondiweruza ine.
16 Ndikadaitana, ndipo akadayankha Iye,Koma sindikadakhulupirira kuti Iye wamvera mau anga,
17 Pakuti andityola ndi mkuntho,Nacurukitsa mabala anga kopanda cifukwa.
18 Sandilola kuti ndipume,Koma andidzaza ndi zowawa.
19 Tikanena za mphamvu, si ndiye wamphamvu?Tikanena za kuweruza, adzamuitana ndani?