22 Kuli cimodzimodzi monsemo, m'mwemo ndikutiIye aononga wangwiro ndi woipa pamodzi.
23 Mkwapulo ukapha modzidzimutsa,Adzaseka tsoka la wosacimwa.
24 Dziko lapansi laperekedwa m'dzanja la woipa;Aphimba maso a oweruza ace.Ngati sindiye, pali yaninso?
25 Tsopano masiku anga afulumira kuposa wamtokoma;Athawa osaona cokoma.
26 Apitirira ngati zombo zaliwiro;Ngati mphungu igudukira cakudya cace.
27 Ndikati, Ndidzaiwala condidandaulitsa,Ndidzasintha nkhope yanga yacisoni, ndidzasekerera;
28 Pamenepo ndiopa zisoni zanga zonse,Ndidziwa kuti simudzandiyesa wosacimwa.