27 Ndikati, Ndidzaiwala condidandaulitsa,Ndidzasintha nkhope yanga yacisoni, ndidzasekerera;
28 Pamenepo ndiopa zisoni zanga zonse,Ndidziwa kuti simudzandiyesa wosacimwa.
29 Mlandu udzanditsutsa;Potero ndigwire nchito cabe cifukwa ninji?
30 Ndikasamba madzi a cipale cofewaNdi kuyeretsa manja anga ndi sopo;
31 Mudzandibviikanso muli zoola,Ndi zobvala zanga zidzanyansidwa nane.
32 Pakuti sindiye munthu, monga ine, kuti ndimyankhe,Kuti tikomane mlandu.
33 Palibe wakutiweruza,Wakutisanjika ife tonse awiri manja ace.