5 Ndiye amene asuntha mapiri, osacidziwa iwo,Amene amagubuduza mu mkwiyo wace.
6 Amene agwedeza dziko lapansi licoke m'malo mwace,Ndi mizati yace injenjemere.
7 Amene alamulira dzuwa ndipo silituruka,Nakomera nyenyezi cizindikilo cakuzitsekera.
8 Woyala thambo yekha,Naponda pa mafunde a panyanja.
9 Wolenga Mlalang'amba, Akamwiniatsatana, ndi Nsangwe,Ndi Kumpotosimpita,
10 Wocita zazikuru zosasanthulika,Ndi zodabwiza zosawerengeka,
11 Taona, Mulungu apita pali ine, koma sindimpenya;Napitirira, koma osamaindikira ine.