21 Ndipo tsiku lopangira Herode anabvala zobvala zacifumu, nakhala pa mpando wacifumu, nawafotokozera iwo mau a pabwalo.
22 Ndipo anthu osonkhanidwawo anapfuula, Ndiwo mau a Mulungu, si a munthu ai.
23 Ndipo pomwepo mngelo wa Ambuye anamkantha, cifukwa sanampatsa Mulungu ulemerero; ndipo anadyedwa ndi mphutsi, natsirizika.
24 Koma mau a Mulungu anakula, nacurukitsa.
25 Ndipo Bamaba ndi Saulo anabwera kucokera ku Yerusalemu m'mene adatsiriza utumiki wao, natenga Yohane wonenedwanso Marko amuke nao.