Macitidwe 10 BL92

Kenturiyo Komeliyo

1 Ndipo kunali munthu ku Kaisareya, dzina lace Komeliyo, kenturiyo wa gulu lochedwa la Italiya,

2 ndiye munthu wopembedza, ndi wakuopa Mulungu ndi banja lace lonse, amene anapatsa anthu zacifundo zambiri, napemphera Mulungu kosaleka.

3 Iye anapenya m'masomphenya poyera, mngelo wa Mulungu alinkudza kwa iye, ngati ora lacisanu ndi cinai la usana, nanena naye, Komeliyo.

4 Ndipo pompenyetsetsa iye ndi kuopa, anati, Nciani, Mbuye? Ndipo anati kwa iye, Mapemphero ako ndi zacifundo zako zinakwera zikhala cikumbutso pamaso pa Mulungu.

5 Ndipo tsopano tumiza amuna ku Y opa, aitane munthu Simoni, wochedwanso Petro;

6 acerezedwa iye ndi wina Simoni wofufuta zikopa, nyumba yace iri m'mbali mwa nyanja.

7 Ndipo m'mene atacoka mngelo amene adalankhula naye, anaitana anyamata ace awiri, ndi msilikari wopembedza, wa iwo amene amtumikira kosaleka;

8 ndipo m'mene adawafotokozerazonse, anawatuma ku Yopa.

9 Koma m'mawa mwace, pokhala paulendo pao iwowa, m'mene anayandikira mudzi, Petro anakwera pachindwi kukapemphera, ngati pa ora lacisanu ndi cimodzi; ndipo anagwidwa njala, nafuna kudya;

10 koma m'mene analikumkonzera cakudya kudamgwera ngati kukomoka;

11 ndipo anaona pathambo padatseguka, ndi cotengera cirinkutsika, conga ngati cinsaru cacikuru, cogwiridwa pa ngondya zace zinai, ndi kutsikira padziko pansi;

12 m'menemo munali nyama za miyendo inai za mitundu yonse, ndi zokwawa za padziko ndi mbalame za m'mlengalenga.

13 Ndipo anamdzera mau, Tauka, Petro; ipha, nudye.

14 Koma Petro anati, Iaitu, Mbuye; pakuti sindinadya ine ndi kale lonse kanthu wamba ndi konyansa.

15 Ndipo mau anamdzeranso nthawi yaciwiri, Cimene Mulungu anayeretsa, usaciyesa cinthu wamba.

16 Ndipo cinacitika katatu ici; ndipo pomwepo cotengeraco cinatengedwa kunka kumwamba.

17 Ndipo pokayika-kayika Petro mwa yekha ndi kuti masomphenya adawaona akuti ciani, taonani, amuna aja otumidwa ndi Komeliyo, atafunsira nyumba ya Simoni, anaima pa cipata,

18 ndipo anaitana nafunsa ngati Simoni, wochedwanso Petro, acerezedwako.

19 Ndipo m'mene Petro analingirira za masomphenya, Mzimu ananena naye, Taona, amuna atatu akufuna iwe.

20 Komatu tauka, nutsike, ndipo upite nao, wosakayika-kayika; pakuti ndawatuma ndine.

21 Ndipo Petro anatsikira kwa anthuwo, nati, Taonani, ine ndine amene mumfuna; cifukwa cace mwadzera nciani?

22 Ndipo anati, Komeliyo kenturiyoyo, munthu wolungama ndi wakuopa Mulungu, amene mtundu wonse wa Ayuda umcitira umboni, anacenjezedwa ndi mngelo woyera kuti atumize nakuitaneni mumuke ku nyumba yace, ndi kummvetsa mau anu.

23 Pamenepo anawalowetsa nawacereza.Ndipo m'mawa mwace ananyamuka naturuka nao, ndi ena a abale a ku Yopaanamperekezaiye.

24 Ndipo m'mawa mwace analowa m'Kaisareya, Koma Komeliyo analikudikira iwo, atasonkhanitsa abale ace ndi mabwenzi ace eni eni.

25 Ndipo panali pakulowa Petro, Komeliyo anakomana naye, nagwa pa mapazi ace, namlambira.

26 Koma Petro anamuutsa iye, nanena, Nyamuka; inenso ndine munthu.

27 Ndipo pakukamba naye, analowa, napeza ambiri atasonkhana;

28 ndipo anati kwa iwo, Mudziwa inu nokha kuti sikuloledwa kwa munthu Myuda adziphatike kapena kudza kwa munthu wa mtundu wina; koma Mulungu anandionetsera ine ndisanenere ali yense ali munthu wamba kapena wonyansa;

29 cifukwa cacenso ndinadza wosakana, m'mene munatuma kundiitana. Pamenepo ndifunsa, mwandiitaniranji?

30 Ndipo Komeliyo anati, Atapita masiku anai, kufikira monga ora ili, ndinalikupemphera m'nyumba yanga pa ora lacisanu ndi cinai; ndipo taonani, padaimirira pamaso panga munthu wobvala cobvala conyezimira,

31 nati Komeliyo, lamveka pemphero lako, ndi zopereka zacifundo zako zakumbukika pamaso pa Mulungu.

32 Cifukwa cace tumiza anthu ku Yopa, akaitane Simoni amene anenedwanso Petro; amene acerezedwa m'nyumba ya Simoni wofufuta zikopa, m'mbali mwa nyanja.

33 Pamenepo ndinatumiza kwa inu osacedwa; ndipo mwacita bwino mwadza kuno, Cifukwa cace taonani tiri tonse pano pamaso pa Mulungu, kumva zonse Ambuye anakulamulirani.

34 Ndipo Petro anatsegula pakamwa pace, nati:Zoona ndizinkidira kuti Mulungu alibe tsankhu;

35 koma m'mitundu yonse, wakumuopa iye ndi wakucita cilungamo alandiridwa naye.

36 Mau amene anatumiza kwa ana a Israyeli, akulalikira Uthenga Wabwino wa mtendere mwa Yesu Kristu (ndiye Ambuye wa onse)

37 mauwo muwadziwa inu, adadzawo ku Yudeya lonse, akuyamba ku Galileya, ndi ubatizo umene Yohane anaulalikira;

38 za Yesu wa ku Nazarete, kuti Mulungu anamdzoza iye ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu; amene anapitapita nacita zabwino, naciritsa onse osautsidwa ndi mdierekezi, pakuti Mulungu anali pamodzi ndi iye.

39 Ndipo ife ndife mboni zazonse adazicita m'dzikola Ayuda ndim'Yerusalemu; amenenso anamupha, nampacika pamtengo,

40 Ameneyo, Mulungu anamuukitsa tsiku lacitatu, nalola kuti aonetsedwe,

41 si kwa anthu onse ai, koma kwa mboni zosankhidwiratu ndi Mulungu, 1 ndiwo ife amene tinadya ndi kumwa naye pamodzi, atauka iye kwa akufa.

42 Ndipo 2 anatilamulira ife tilalikire kwa anthu, ndipo ticite umboni kuti 3 Uyu ndiye amene aikidwa ndi Mulungu akhale woweruza amoyo ndi akufa.

43 4 Ameneyu aneneri onse amcitira umboni, kuti onse akumkhulupirira iye adzalandira cikhululukiro ca macimo ao, mwa dzina lace.

44 Petro ali cilankhulire, 5 Mzimu Woyera anagwa pa onse akumva mauwo.

45 Ndipo 6 anadabwa okhulupirirawo akumdulidwe onse amene anadza ndi Petro, cifukwa pa 7 amitundunso panathiridwa mphatso ya Mzimu Woyera.

46 Pakuti anawamva iwo alikulankhula ndi malilime, ndi kumkuza Mulungu. Pamenepo Petro anayankha,

47 Kodi pali munthu akhoza kuletsa madzi, kuti asabatizidwe awa, amene alandira Mzimu Woyera 8 ngatinso ife?

48 Ndipo analamulira iwo 9 abatizidwe m'dzina la Yesu Kristu, Pamenepo anampempha iye atsotse masiku.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28