Macitidwe 6 BL92

Asankha atumiki asanu ndi awiri

1 Koma masiku awo, pakucurukitsa ophunzira, kunauka cidandaulo, Aheleniste kudandaula pa Ahebri, popeza amasiye ao anaiwalika pa citumikiro ca tsiku ndi tsiku.

2 Ndipo khumi ndi awiriwo anaitana unyinji wa ophunzira, nati, Sikuyenera kuti ife tisiye mau a Mulungu ndi kutumikira podyerapo.

3 Cifukwa cace, abale, yang'anani mwa inu amuna asanu ndi awiri a mbiri yahwino, odzala ndi Mzimu ndi nzeru, amene tikawaike asunge nchito iyi.

4 Koma ife tidzalimbika m'kupemphera, ndi kutumikira mau.

5 Ndipo mau amene anakonda unyinji wonse; ndipo anasankha Stefano, ndiye munthu wodzala ndi cikhulupiriro ndi Mzimu Woyera, ndi Filipo, ndi Prokoro, ndi Nikanora ndi Timo, ndi Parmena, ndi Nikolao, ndiye wopinduka wa ku Antiokeya:

6 amenewo anawaika pamasopa atumwi; ndipo m'mene adapemphera, anaika manja pa iwo.

7 Ndipo mau a Mulungu anakula; ndipo ciwerengero ca akuphunzira cidacurukatu ku Yerusalemu; ndipo khamu lalikuru la ansembe linamvera cikhulupiriroco.

Stefano woyamba wophedwa cifukwa ca Kristu

8 Ndipo Stefano, wodzala ndi cisomo ndi mphamvu, anacita zozizwa ndi zizindikilo zazikuru mwa anthu.

9 Koma anauka ena a iwo ocokera m'sunagoge wa Alibertino, ndi Akurenayo, ndi Aalesandreyo, ndi mwa iwo a ku Kilikiya ndi ku Asiya, natsutsana ndi Stefano.

10 Ndipo sanathe kuilaka nzeru ndi Mzimu amene analankhula naye.

11 Pamenepo anafuna anthu akumpitira pansi, ndi kuti, Tidamumva iye alikunenera Mose ndi Mulungu mau amwano.

12 Ndipo anautsa anthu, ndi akuru, ndi alembi, namfikira, namgwira iye, nadza naye ku bwalo la akulu,

13 naimika mboni zonama, zakunena, Munthu ameneyo saleka kunenera malo oyera amene, ndi cilamulo;

14 pakuu tinamumva iye alikunena, kuti, Yesu Mnazarayo amene adzaononga malo ano, nadzasanduliza miyambo imene Mose anatipatsa.

15 Ndipo anampenyetsetsa onse akukhala m'bwalo la akulu, naona nkhope yace ngati nkhope ya mnaelo.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28