Macitidwe 18 BL92

Paulo ku Korinto ndi ku Efeso, Abwera ku Yerusalemu

1 Zitapita izi anacoka ku Atene, nadza ku Korinto.

2 Ndipo anapeza Myuda wina dzina lace Akula, pfuko lace la ku Ponto, atacoka catsopano ku Italiya, pamodzi ndi mkazi wace Priskila, cifukwa Klaudiyo analamulira Ayuda onse acoke m'Roma; ndipo Pauloanadza kwa iwo:

3 ndipo popeza anali wa nchito imodzimodzi, anakhala nao, ndipo iwowa anagwira nchito; pakuti nchito yao inali yakusoka mahema.

4 Ndipo anafotokozera m'sunagogemasabata onse, nakopa Ayuda ndi Ahelene.

5 Koma pamene Sila ndi Timoteo anadza potsika ku Makedoniya, Paulo anapsinjidwa ndi mau, nacitira umboni kwa Ayuda kuti Yesu ndiye Kristu.

6 Koma pamene iwo anamkana, nacita mwano, anakutumula maraya ace, nati kwa iwo, Mwazi wanu ukhale pa mitu yanu; ine ndiribe kanthu; kuyambira tsopano ndinka kwa amitundu.

7 Ndipo anacoka kumeneko, nalowa m'nyumba ya munthu, dzina lace Tito Yusto, amene anapembedza Mulungu, nyumba yace inayandikizana ndi sunagoge.

8 Ndipo Krispo, mkuru wasunagoge, anakhulupirira Ambuye, ndi apabanja ace onse; ndipo Akorinto ambiri anamva, nakhulupira, nabatizidwa.

9 Ndipo Ambuye anati kwa Paulo usiku m'masomphenya, Usaope, koma nena, usakhale cete;

10 cifukwa Ine ndiri pamodzi ndi iwe, ndipo palibe munthu adzautsana ndi iwe kuti akuipse; cifukwa ndiri nao anthu ambiri m'mudzi muno.

11 Ndipo anakhala komwe caka cimodzi kudza miyezi isanu ndi umodzi; naphunzitsamau a Mulungu mwa iwo.

12 Tsono pamene Galiyo anali ciwanga ca Akaya, Ayuda ndi mtima umodzi anamuukira Paulo, nanka naye ku mpando wa ciweruziro,

13 kuti, Uyu akopa anthu apembedze Mulungu pokana cilamulo.

14 Koma pamene Paulo anati atsegule pakamwa pace, Galiyo anati kwa Ayuda, Ukadakhala mlandu wa cosalungama, kapena dumbo loipa, Ayuda inu, mwenzi nditakumverani inu;

15 koma akakhala mafunso a mau ndi maina ndi cilamulo canu; muyang'ane inu nokha; sindifuna kuweruza zimenezi.

16 Ndipo anawapitikitsa pa mpando wa ciweruziro.

17 Ndipo anamgwira Sostene, mkuru wa sunagoge, nampanda ku mpando wa ciweruziro. Ndipo Galiyo sanasamalira zimenezi.

18 Paulo atakhala cikhalire masiku ambiri, anatsazika abale, nacoka pamenepo, napita m'ngalawa ku Suriya, pamodzi naye Priskila ndi Akula; popeza anameta mutu wace m'Kenkreya; pakuti adawinda.

19 Ndipo iwo anafika ku Efeso, ndipo iye analekana nao pamenepo: koma iye yekha analowa m'sunagoge, natsutsana ndi Ayuda.

20 Pamene iwo anamfunsa iye kuti akhale nthawi yina yoenjezerapo, sanabvomereza;

21 koma anawatsazika, nati, Akafuna Mulungu, ndidzabwera kwa inu; ndipo anacoka ku Efeso m'ngalawa.

22 Ndipo pamene anakoceza pa Kaisareya, anakwera nalankhulana nao Mpingo, natsikira ku Antiokeya.

23 Atakhala kumeneko nthawi, anacoka, napita pa dziko la Galatiya ndi Frugiya m'dziko m'dziko, nakhazikitsaakuphunzira onse.

Apolo ku Efeso ndi Korinto

24 Ndipo anafika ku Efeso Myuda wina dzina lace Apolo, pfuko lace la ku Alesandreya, munthu wolankhula mwanzeru; ndipo anali wamphamvu m'malembo.

25 Iyeyo aoaphunzitsidwa m'njira ya Ambuye; pokhala nao mzimu wacangu, ananena ndi kuphunzitsa mosamalira zinthu za Yesu, ndiye wodziwa ubatizo wa Yohane wokha;

26 ndipo iye anayamba kulankhula molimba mtima m'sunagoge, koma pamene anamumva iye Priskila ndi Akula, anamtenga, namfotokozera njira ya Mulungu mosamalitsa.

27 Ndipo pamene iye anafuna kuoloka kunka ku Akaya, abale anamfulumiza, ndi kulembera akalata kwa akuphunzira kuti amlandire: ndipo pamene anafika, iye anathangata ndithu iwo akukhulupira mwa cisomo;

28 pakuti ndi mphamvu anatsutsa Ayuda, pamaso pa anthu, nasonyeza mwa malembo kuti Yesu ndiye Kristu.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28