29 kuti musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.
30 Tsono pamene iwo anamuka anatsikira ku Antiokeya; ndipo anasonkhanitsa khamu, napereka kalatayo.
31 Pamene anawerenga, anakondwera cifukwa ca cisangalatso cace.
32 Ndipo Yuda ndi Sila, okhala eni okha aneneri, anasangalatsa abale ndi mau ambiri, nawalimbikitsa.
33 Pamene anakhala nthawi, abale analawirana nao ndi mtendere amuke kwa iwo amene anawatumiza. [
34 ]
35 Koma Paulo ndi Bamaba anakhalabe m'Antiokeya, nalinkuphunzitsa, ndi kulalikira mau a Ambuye pamodzi ndi ena ambiri.