32 Ndipo Yuda ndi Sila, okhala eni okha aneneri, anasangalatsa abale ndi mau ambiri, nawalimbikitsa.
33 Pamene anakhala nthawi, abale analawirana nao ndi mtendere amuke kwa iwo amene anawatumiza. [
34 ]
35 Koma Paulo ndi Bamaba anakhalabe m'Antiokeya, nalinkuphunzitsa, ndi kulalikira mau a Ambuye pamodzi ndi ena ambiri.
36 Patapita masiku, Paulo anati kwa Bamaba, Tibwerenso, tizonde abale m'midzi yonse m'mene tinalalikiramo mau a Ambuye, tione mkhalidwe wao.
37 Ndipo Bamaba anafuna kumtenga Yohane uja, wochedwa Marko.
38 Koma sikunamkomera Paulo kumtenga iye amene anawasiya nabwerera pa Pamfuliya paja osamuka nao kunchito.