22 Amuna inu Aisrayeli, mverani mau awa: Yesu Mnazarayo, mwamuna wocokera kwa Mulungu, wosonyezedwa kwa inu ndizimphamvu, ndi zozizwa, ndi zizindikilo, zimene Mulungu anazicita mwa iye pakati pa inu, monga mudziwa nokha;
23 ameneyo, woperekedwa ndi uphungu woikidwa ndi kudziwiratu kwa Mulungu, inu mwampacika ndi kumupha ndi manja a anthu osayeruzika;
24 yemweyo Mulungu anamuukitsa, atamasula zowawa za imfa, mwakuti sikunali kotheka kuti iye agwidwe nayo.
25 Pakuti Davine anena za Iye,Ndinaona Mbuye pamaso panga nthawi zonse;Cifukwa ali pa dzanja langa lamanja, kuti ndingasinthike;
26 Mwa ici unakondwera mtima wanga, ndipo linasangalala lilime langa;Ndipo thupi langanso lidzakhala m'ciyembekezo.
27 Pakuti simudzasiya moyo wanga ku Hade,Kapena simudzapereka Woyera wanu aone cibvunde,
28 Munandidziwitsa ine njira za moyo;Mudzandidzaza ndi kukondwera pamaso panu.