2 Ndipo ansembe akulu ndi akulu a Ayuda ananenera Paulo kwa iye; ndipo iwo anamdandaulira,
3 nampempha kuti mlandu wace wa Paulo uipe, kuti amuitane iye adze ku Yerusalemu; iwo amcitira cifwamba kuti amuphe panjira.
4 Pamenepo Festo anayankha, kuti Paulo asungike ku Kaisareya, ndi kuti iye mwini adzapitako posacedwa.
5 Cifukwa cace, ati, iwo amene akhoza mwa inu amuke nane potsikirako, ndipo ngati kuli kanthu kosayenera mwa munthuyo amnenere iye.
6 Ndipo m'mene adatsotsa mwa iwo masiku asanu ndi atatu kapena khumi okha anatsikiraku Kaisareya; ndipo m'mawa mwace anakhala pa mpando waciweruziro, nalamulira kuti atenge Paulo.
7 Ndipo m'mene anafika iye, Ayuda adatsikawo ku Yerusalemu anaimirira pomzinga iye, namnenera zifukwa zambiri ndi zazikuru, zimene sanakhoza kuzitsimikiza;
8 koma Paulo podzikanira ananena, Sindinacimwa kanthu kapena pacilamulo, kapena paKacisi, kapena pa Kaisara.