18 nathira manja atumwi, nawaika m'ndende ya anthu wamba.
19 Koma mngelo wa Ambuye anatsegula pakhomo pa ndende usiku, nawaturutsa, nati,
20 Pitani, ndipo imirirani, nimulankhule m'Kacisi kwa anthu onse mau a Moyo umene.
21 Ndipo atamva ici, analowa m'Kacisi mbanda kuca, naphunzitsa. Koma anadza mkulu wa ansembe ndi iwo amene analinaye, nasonkhanitsa a bwalo la akuru, ndi akulu onse a ana a Israyeli, natuma kundende atengedwe ajawo.
22 Koma anyamata amene adafikako sanawapeza m'ndende, ndipo pobwera anafotokoza,
23 nanena, Nyumba yandende tinapeza citsekere, ndi alonda alikuimirira pamakomo; koma pamene tinatsegula sitinapezamo mmodzi yense.
24 Koma m'mene anamva mau awa mdindo wa Kacisi ndi ansembe akulu anathedwa nzeru ndi iwo aja, kuti ici cidzatani.